Mateyu 25:9-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Koma ocenjera anayankha nati, Kapena sangakwanire ife ndi inu; koma makamaka mukani kwa ogulitsa malonda, mukadzigulire inu nokha.

10. Ndipo pamene iwo analikumuka kukagula, mkwati anafika; ndipo okonzekawo, analowa naye pamodzi muukwati; ndipo anatseka pakhomo.

11. Koma pambuyo pace anadzanso anamwali enawo, nati, Mbuye, Mbuye, mutitsegulire ife.

12. Koma iye anayankha nati, Indetu ndinena kwa inu, sindikudziwani.

13. Cifukwa cace dikirani, pakuti simudziwa tsiku lace, kapena nthawi yace.

Mateyu 25