1. Ndipo parnene iwo anayandikira ku Yerusalemu, nafika ku Betefage, ku phiri la Azitona, pamenepo Yesu anatumiza ophunzira awiri,
2. nanena kwa iwo, Mukani ku mudzi wopenyana ndi inu, ndipo pomwepo mudzapeza buru womangidwa, ndi mwana wace pamodzi nave, masulani iwo, mudze nao kwa Ine.
3. Ndipo munthu akanena kanthu ndi inu, mudzati, Ambuye asowa iwo, Ndipo pomwepo adzawatumiza.
4. Ndipo ici cinatero, kuti cikacitidwe conenedwa ndi mneneri kuti,
5. Tauzani mwanawamkazi wa Ziyoni,Taona, Mfumu yako idza kwa iwe,Wofatsa ndi wokwera pa buru,Ndi pa kaburu, mwana wa nyama yonyarnula katundu.
6. Ndipo ophunzirawo anamuka, nacita monga Yesu anawauza;
7. nabwera ndi buru ndi mwana wace, naika pa iwo zobvala zao, nakhala Iye pamenepo.
8. Ndipo ambirimbiri a mpingowo anayala zobvala zao panjira; Ndipo ena anadula nthambi za mitengo, naziyala m'njirarno.