Mateyu 20:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pakuti Ufumu wa Kumwamba ufanana ndi munthu mwini banja, amene anaturuka mamawa kuka lembera anchito a m'munda wace wampesa.

2. Ndipo parnene adapangana ndi anchito, pa rupiya latheka limodzi tsiku limodzi, anawatumiza ku munda wace.

3. Ndipo anaturuka dzuwa litakwera, naona ena ataima cabe pabwalo;

4. ndipo kwa iwo anati, Pitani inunso kumunda, ndipo ndidzakupatsani cimene ciri coyenera. Ndipo iwo anapita.

5. Ndiponso anaturuka usana, ndimonso popendeka dzuwa, nacita cimodzimodzi.

Mateyu 20