5. Koma inu munena, Amene ali yense anena kwa atate wace kapena kwa amace, Ico ukanathandizidwa naco, neoperekedwa kwa Mulungu;
6. iyeyo sadzalemekeza atate wace. Ndipo inu mupeputsa mau a Mulungu cifukwa ca miyambo yanu.
7. Onyenga inu! Yesaya ananenera bwino za inu, ndikuti,
8. Anthu awa andilemekeza Ine ndi milomo yao;Koma mtima wao uli kutari ndi Ine.