Mateyu 15:3-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndipo Iye anayankha, nati kwa iwo, Inunso mulumphiranji lamulo la Mulungu cifukwa ca miyambo yanu?

4. Pakuti Mulungu anati,Lemekeza atate wako ndi amako; ndipo,Wakunenera atate wace ndi amace zoipa, afe ndithu.

5. Koma inu munena, Amene ali yense anena kwa atate wace kapena kwa amace, Ico ukanathandizidwa naco, neoperekedwa kwa Mulungu;

6. iyeyo sadzalemekeza atate wace. Ndipo inu mupeputsa mau a Mulungu cifukwa ca miyambo yanu.

7. Onyenga inu! Yesaya ananenera bwino za inu, ndikuti,

8. Anthu awa andilemekeza Ine ndi milomo yao;Koma mtima wao uli kutari ndi Ine.

9. Koma andilambira Ine kwacabe,Ndi kuphunzitsa maphunzitso, malangizo a anthu.

10. Ndipo Iye anaitana makamuwo nati kwa iwo, Imvani, nimudziwitse;

11. si cimene cilowa m'kamwa mwace ciipitsa munthu; koma cimene cituruka m'kamwa mwace, ndico ciipitsa munthu.

12. Pomwepo anadza ophunzira, nanena kwa Iye, Mudziwa kodi kuti Afarisi anakhumudwa pakumva conenaco?

Mateyu 15