1. Pomwepo anadza kwa Yesu Afarisi ndi alembi, ocokera ku Yerusalemu, nati,
2. Ophunzira anu alumphiranji miyambo ya makolo? pakuti sasamba manja pakudya.
3. Ndipo Iye anayankha, nati kwa iwo, Inunso mulumphiranji lamulo la Mulungu cifukwa ca miyambo yanu?
4. Pakuti Mulungu anati,Lemekeza atate wako ndi amako; ndipo,Wakunenera atate wace ndi amace zoipa, afe ndithu.
5. Koma inu munena, Amene ali yense anena kwa atate wace kapena kwa amace, Ico ukanathandizidwa naco, neoperekedwa kwa Mulungu;
6. iyeyo sadzalemekeza atate wace. Ndipo inu mupeputsa mau a Mulungu cifukwa ca miyambo yanu.
7. Onyenga inu! Yesaya ananenera bwino za inu, ndikuti,