25. Ndipo pa ulonda wacinai wa usiku, Iye anadza kwa iwo, nayenda pamwamba pa nyanja.
26. Koma m'mene ophunzirawo anamuona Iye, alikuyenda pamadzi, ananthunthumira, nati, ndi mzukwa! Ndipo anapfuula ndi mantha.
27. Koma pomwepo Yesu analankhula nao, nati, Limbani mtima; ndine; musaope.
28. Ndipo Petro anamyankha Iye nati, Ambuye, ngati ndinutu, mundiuze ndidze kwa lou pamadzi.