Mateyu 12:5-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Kapena simunawerenga kodi m'cilamulo, kuti tsiku la Sabata ansembe m'Kacisi amaipitsa tsiku la Sabata, nakhala opanda cimo?

6. Koma ndinena kwa inu, kuti wakuposa Kacisiyo ali pompano.

7. Koma mukadadziwa nciani ici:Ndifuna cifundo, si nsembe ai; simukadaweruza olakwa iwo osacimwa,

8. pakuti Mwana wa munthu ali mwini tsiku la Sabata.

9. Ndipo Iye anacokera pamenepo, nalowa m'sunagoge mwao;

Mateyu 12