Masalmo 99:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Yehova ndiye mfumu; mitundu ya anthu injenjemere;Iye akhala pakati pa akerubi; dziko lapansi ligwedezeke.

2. Yehova ndiye wamkuru m'Ziyoni;Ndipo akwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.

3. Alemekeze dzina lanu lalikuru ndi loopsa;Ili ndilo loyera.

4. Ndipo mphamvu ya mfumu ikonda ciweruzo;Inu mukhazikitsa zolunjika,Mucita ciweruzo ndi cilungamo m'Yakobo.

Masalmo 99