7. Mpatseni Yehova, inu, mafuko a mitundu ya anthu,Mpatseni Yehova ulemerero ndi mphamvu,
8. Mpatseni Yehova ulemerero wa dzina lace;Bwerani naco copereka, ndipo fikani ku mabwalo ace.
9. Gwadirani Yehova moyera ndi mokometsetsa:Njenjemerani pamaso pace, inu dziko lonse lapansi.