Masalmo 96:7-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Mpatseni Yehova, inu, mafuko a mitundu ya anthu,Mpatseni Yehova ulemerero ndi mphamvu,

8. Mpatseni Yehova ulemerero wa dzina lace;Bwerani naco copereka, ndipo fikani ku mabwalo ace.

9. Gwadirani Yehova moyera ndi mokometsetsa:Njenjemerani pamaso pace, inu dziko lonse lapansi.

Masalmo 96