6. Adaniwo atha psiti, apululuka nthawi zonse;Ndipo midziyo mwaipasula,Cikumbukilo cao pamodzi catha.
7. Koma Yehova akhala cikhalire:Anakonzeratu mpando wacifumu wace kuti aweruze.
8. Ndipo Iyeyu adzaweruza dziko lapansi m'cilungamo,Nadzaweruza anthu molunjika.