Masalmo 89:19-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Pamenepo munalankhula m'masompenya ndi okondedwa anu,Ndipo mudati, Ndasenza thandizo pa ciphona;Ndakweza wina wosankhika mwa anthu.

20. Ndapeza Davide mtumiki wanga;Ndamdzoza mafuta anga oyera.

21. Amene dzanja langa lidzakhazikika naye;Inde mkono wanga udzalimbitsa.

22. Mdani sadzamuumira mtima;Ndi mwana wa cisalungamo sadzamzunza.

23. Ndipo ndidzaphwanya omsautsa pamaso pace;Ndidzapandanso odana naye.

24. Koma cikhulupiriko canga ndi cifundo canga zidzakhala naye;Ndipo nyanga yace idzakwezeka m'dzina langa.

25. Ndipo ndidzaika dzanja lace panyanja,Ndi dzanja lamanja lace pamitsinje.

Masalmo 89