18. Pakuti cikopa cathu cifuma kwa Yehova;Ndi mfumuyathu kwa Woyera wa Israyeli.
19. Pamenepo munalankhula m'masompenya ndi okondedwa anu,Ndipo mudati, Ndasenza thandizo pa ciphona;Ndakweza wina wosankhika mwa anthu.
20. Ndapeza Davide mtumiki wanga;Ndamdzoza mafuta anga oyera.