Masalmo 89:18-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Pakuti cikopa cathu cifuma kwa Yehova;Ndi mfumuyathu kwa Woyera wa Israyeli.

19. Pamenepo munalankhula m'masompenya ndi okondedwa anu,Ndipo mudati, Ndasenza thandizo pa ciphona;Ndakweza wina wosankhika mwa anthu.

20. Ndapeza Davide mtumiki wanga;Ndamdzoza mafuta anga oyera.

Masalmo 89