Masalmo 86:6-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Cherani khutu pemphero langa, Yehova;Nimumvere mau a kupemba kwanga,

7. Tsiku la msauko wanga ndidzaitana Inu;Popeza mudzandibvomereza.

8. Pakati pa milungu palibe wina wonga Inu, Ambuye;Ndipo palibe nchito zonga zanu.

9. Amitundu onse mudawalenga adzadza nadzagwada pamaso panu, Ambuye; Nadzalemekeza dzina lanu.

10. Pakuti Inu ndinu wamkulu, ndi wakucita zodabwiza;Inu ndinu Mulungu, nokhanu.

11. Mundionetse njira yanu, Yehova; ndidzayenda m'coonadi canu:Muumbe mtima wanga ukhale umodzi kuti uliope dzina lanu.

Masalmo 86