Masalmo 83:7-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Gebala ndi Amoni ndi Amaleki;Filistiya, pamodzi ndi iwo okhala m'Turo.

8. Asuri anaphatikana nao;Anakhala dzanja la ana a Loti,

9. Muwacitire monga munacitira Midyani;Ndi Sisera, ndi Jabini ku mtsinje wa Kisoni:

10. Amene anaonongeka ku Endoro;Anakhala ngati ndowe ya kumunda.

11. Muwaike akulu ao ngati Orebu ndi Zeebu;Mafumu ao ngati Zeba ndi Zalimuna:

12. Amene anati, TilandeMalo okhalamo Mulungu, akhale athu.

13. Mulungu wanga, muwaike akhale ngati mungu;Ngati ziputu zomka ndi mphepo.

14. Monga moto upsereza nkhalango,Ndi monga lawi liyatsa mapiri;

Masalmo 83