Masalmo 80:4-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Yehova, Mulungu wa makamu,Mudzakwiyira pemphero la anthu anu kufikira liti?

5. Munawadyetsa mkate wa misozi,Ndipo munawamwetsa misozi yambiri.

6. Mutiika kuti atilimbirane anzathu;Ndipo adani athu atiseka mwa iwo okha,

7. Mulungu wa makamu, mutibweze;Nimuwalitse nkhope yanu, ndipo tidzapulumuka.

8. Mudatenga mpesa kucokera ku Aigupto:Munapitikitsa amitundu ndi kuuoka uwu.

9. Mudasoseratu pookapo,Idagwiritsa mizu yace, ndipo unadzaza dziko.

Masalmo 80