60. Ndipo anacokera cokhalamo ca ku Silo,Cihemaco adacimanga mwa anthu;
61. Napereka mphamvu yace m'ukapolo,Ndi ulemerero wace m'dzanja la msautsi.
62. Naperekanso anthu ace kwa lupanga;Nakwiya naco colandira cace.
63. Moto unapsereza anyamata ao;Ndi anamwali ao sanalemekezeka.
64. Ansembe ao anagwa ndi lupanga;Ndipo amasiye ao sanacita maliro.
65. Pamenepo Ambuye anauka ngati wam'tulo;Ngati ciphona cakucita nthungululu ndi vinyo.