38. Koma Iye pokhala ngwa cifundo,Anakhululukira coipa, osawaononga;Nabweza mkwiyo wace kawiri kawiri,Sanautsa ukali wace wonse.
39. Ndipo anakumbukira kuti iwo ndiwo anthu;Mphepo yopita yosabweranso.
40. Kawiri kawiri nanga anapikisana ndi Iye kucigwako,Nammvetsa cisoni m'cipululu.
41. Pakuti anabwerera m'mbuyo, nayesa Mulungu,Nacepsa Woyerayo wa Israyeli.
42. Sanakumbukila dzanja lace,Tsikuli anawaombola kwa msautsi.