Masalmo 78:34-42 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

34. Pamene anawapha ndipo anamfuna Iye;Nabwerera, nafunitsitsa Mulungu,

35. Ndipo anakumbukila kuti Mulungu ndiye thanthwe lao,Ndi Mulungu Wam'mwambamwamba Mombolo wao.

36. Koma anamsyasyalika pakamwa pao,Namnamiza ndi lilime lao.

37. Popeza mtima wao sunakonzekera Iye,Ndipo sanakhazikika m'cipangano cace.

38. Koma Iye pokhala ngwa cifundo,Anakhululukira coipa, osawaononga;Nabweza mkwiyo wace kawiri kawiri,Sanautsa ukali wace wonse.

39. Ndipo anakumbukira kuti iwo ndiwo anthu;Mphepo yopita yosabweranso.

40. Kawiri kawiri nanga anapikisana ndi Iye kucigwako,Nammvetsa cisoni m'cipululu.

41. Pakuti anabwerera m'mbuyo, nayesa Mulungu,Nacepsa Woyerayo wa Israyeli.

42. Sanakumbukila dzanja lace,Tsikuli anawaombola kwa msautsi.

Masalmo 78