Masalmo 78:22-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Popeza sanakhulupirira Mulungu,Osatama cipulumutso cace.

23. Koma analamulira mitambo iri m'mwamba,Natsegula m'makomo a kumwamba.

24. Ndipo anawabvumbitsira mana, adye,Nawapatsa tirigu wa kumwamba.

25. Yense anadya mkate wa omveka:Anawatumizira cakudya cofikira,

26. Anaombetsa m'mwamba mphepo ya kum'mawa:Natsogoza mwela ndi mphamvu yace.

27. Ndipo anawabvumbitsira nyama ngati pfumbi,Ndi mbalame zouluka ngati mcenga wa kunyanja:

28. Ndipo anazigwetsa pakati pa misasa yao,Pozungulira pokhala iwo.

29. Potero anadya nakhuta kwambiri;Ndipo anawapatsa cokhumba iwo.

Masalmo 78