Masalmo 78:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Tamverani, anthu anga, cilamulo canga;Cherezani khutu lanu mau a pakamwa panga.

2. Ndidzatsegula pakamwa panga mofanizira;Ndidzachula zinsinsi zoyambira kale;

3. Zimene tinazimva, ndi kuzidziwa,Ndipo makolo athu anatifotokozera.

4. Sitidzazibisira ana ao,Koma kufotokozera mbadwo ukudzawo zolemekeza za Yehova,Ndi mphamvu yace, ndi zodabwiza zace zimene anazicita.

Masalmo 78