Masalmo 77:9-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Kodi Mulungu waiwala kucita cifundo?Watsekereza kodi nsoni zokoma zace mumkwiyo?

10. Ndipo ndinati, Cindilaka ici;Koma ndikumbukila zaka za dzanja lamanja la Wam'mwambamwamba.

11. Ndidzakumbukila zimene adazicita Ambuye;Inde, ndidzakumbukila zodabwiza zanu zoyambira kale.

12. Ndipo ndidzalingalira nchito yanu yonse,Ndi kulingalirabe zimene munazicita Inu.

13. Mulungu, m'malo opatulika muli njira yanu;Mulungu wamkuru ndani monga Mulungu?

14. Inu ndinu Mulungu wakucita codabwiza;Munazindikiritsa mphamvu yanu mwa mitundu ya anthu.

15. Munaombola anthu anu ndi mkonowanu,Ndiwo ana a Yakobo, ndi a Yosefe.

16. Madziwo anakuonani Mulungu;Anakuonani madziwo; anacita mantha:Zozama zomwe zinanjenjemera,

17. Makongwa anatsanula madzi;Thambo lidamvetsa liu lace;Mibvi yanu yomwe inaturukira.

18. Liu la bingu lanu linatengezanatengezana;Mphezi zinaunikira ponse pali anthu;Dziko lapansi linanjenjemera ndi kugwedezeka.

Masalmo 77