Masalmo 77:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndidzapfuulira kwa Mulungu ndi mau anga;Kwa Mulungu ndi mau anga, ndipo adzandicherezera khutu.

2. Tsiku la nsautso yanga ndinafuna Ambuye:Dzanja langa linatambalika usiku, losaleka;Mtima wanga unakanakutonthozedwa.

3. Ndikumbukila Mulungu ndipo ndibvutika;Ndilingalira ndipo mzimu wanga ukomoka.

Masalmo 77