4. Inu ndinu wakuunikira, ndi womveka wakuposa mapiri muli acifwamba.
5. Olimba mtima cifunkhidwa cuma cao, agona tulo tao;Amuna onse amphamvu asowa manja ao.
6. Pa kudzudzula kwanu, Mulungu wa Yakobo,Gareta ndi kavalo yemwe anagwa m'tulo.
7. Inu ndinu woopsa;Ndipo utauka mkwiyo wanu adzakhala ciriri ndani pamaso panu?
8. Mudamveketsa ciweruzo cocokera Kumwamba;Dziko lapansi linacita mantha, nilinakhala cete,
9. Pakuuka Mulungu kuti aweruze,Kuti apulumutse ofatsa onse a pa dziko lapansi.