1. Mulungu, munatitayiranji citayire?Mkwiyo wanu ufukiranji pa nkhosa za kubusa kwanu?
2. Kumbukilani msonkhano wanu, umene munaugula kale,Umene munauombola ukhale pfuko la colandira canu;Phiri La Ziyoni limene mukhalamo.
3. Nyamulani mapazi anu kukapenya mapasukidwe osatha,Zoipa zonse adazicita mdani m'malo opatulika.