Masalmo 73:25-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Ndiri ndi yani Kumwamba, koma Inu?Ndipo Pa dziko lapansi palibe wina wondikonda koma Inu.

26. Likatha thupi langa ndi mtima wanga:Mulungu ndiye thanthwe la mtima wanga, ndi colandira canga cosatha.

27. Pakuti, taonani, iwo okhala patali ndi Inu adzaonongeka;Muononga onse akupembedza kwina, kosiyana ndi Inu.

28. Koma ine, kundikomera kuyandikiza kwa Mulungu:Ndimuyesa Ambuye Yehova pathawirapo ine,Kuti ndifotokozere nchito zanu zonse,

Masalmo 73