Masalmo 73:12-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Tapenyani, oipa ndi awa;Ndipo pokhazikika cikhazikikire aonjezerapo pa cuma cao.

13. Indedi, ndinayeretsa mtima wanga kwacabe,Ndipo ndinasamba m'manja mosalakwa;

14. Popeza andisautsa tsiku lonse,Nandilanga mamawa monse,

15. Ndikadati, Ndidzafotokozera cotere,Taonani, ndikadacita cosakhulupirika ndi mbadwo wa ana ako.

16. Pamene ndinayesa kudziwitsa ici,Ndinabvutika naco;

17. Mpaka ndinalowa m'zoyera za Mulungu,Ndi kulingalira citsiriziro cao.

Masalmo 73