Masalmo 69:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipulumutseni Mulungu;Pakuti madzi afikira moyo wanga.

2. Ndamira m'thope lozama, lopanda poponderapo;Ndalowa m'madzi ozama, ndipo cigumula candimiza.

3. Ndalema ndi kupfuula kwanga; kum'mero kwauma gwa:M'maso mwanga mwada poyembekeza Mulungu wanga.

4. Ondida kopanda cifukwa acuruka koposa tsitsi la pamutu panga;Ofuna kunditha, ndiwo adani anga monama, ali ndi mphamvu:Pamenepo andibwezetsa cosafunkha ine.

Masalmo 69