23. Kuti ubviike phazi lako m'mwazi,Kuti malilime a agaru ako alaweko adani ako.
24. Anapenya mayendedwe anu, Mulungu,Mayendedwe a Mulungu wanga, Mfumu yanga, m'malo oyera.
25. Oyimbira anatsogolera, oyimba zoyimba anatsata m'mbuyo,Pakatipo anamwali oyimba mangaka.
26. Lemekezani Mulungu m'masonkhano,Ndiye Ambuye, inu a gwero la Israyeli.
27. Apo pali Benjamini wamng'ono, wakuwacita ufumu,Akuru a Yuda, ndi a upo wao,Akulu a Zebuloni, akulu a Naftali.
28. Mulungu wako analamulira mphamvu yako:Limbitsani, Mulungu, cimene munaticitira.