1. Auke Mulungu, abalalike adani ace;Iwonso akumuda athawe pamaso pace.
2. Muwacotse monga utsi ucotseka; Monga phula lisungunuka pamoto,Aonongeke oipa pamaso pa Mulungu.
3. Koma olungama akondwere; atumphe ndi cimwemwe pamaso pa Mulungu;Ndipo asekere naco cikondwerero.