Masalmo 66:6-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Anasanduliza nyanja ikhale mtunda:Anaoloka mtsinje coponda pansi:Apo tinakondwera mwa Iye.

7. Acita ufumu mwa mphamvu yace kosatha;Maso ace ayang'anira amitundu;Opikisana ndi Iye asadzikuze.

8. Lemekezani Mulungu wathu, mitundu ya anthu inu,Ndipo mumveketse liu la cilemekezo cace:

9. Iye amene asunga moyo wathu tingafe,Osalola phazi lathu literereke.

10. Pakati munatiyesera, Mulungu:Munatiyenga monga ayenga siliya.

11. Munapita nafe kuukonde;Munatisenza cothodwetsa pamsana pathu.

Masalmo 66