6. Anasanduliza nyanja ikhale mtunda:Anaoloka mtsinje coponda pansi:Apo tinakondwera mwa Iye.
7. Acita ufumu mwa mphamvu yace kosatha;Maso ace ayang'anira amitundu;Opikisana ndi Iye asadzikuze.
8. Lemekezani Mulungu wathu, mitundu ya anthu inu,Ndipo mumveketse liu la cilemekezo cace:
9. Iye amene asunga moyo wathu tingafe,Osalola phazi lathu literereke.
10. Pakati munatiyesera, Mulungu:Munatiyenga monga ayenga siliya.
11. Munapita nafe kuukonde;Munatisenza cothodwetsa pamsana pathu.