1. Imvani Yehova, mau anga, m'kudandaula kwanga;Sungani moyo wanga angandiopse mdani.
2. Ndibiseni pa upo wacinsinsi wa ocita zoipa;Pa phokoso la ocita zopanda pace:
3. Amene anola lilime lao ngati lupanga,Napiringidza mibvi yao, ndiyo mau akuwawitsa;
4. Kuponyera wangwiro mobisika:Amponyera modzidzimutsa, osaopa.