7. Apitetu ngati madzi oyenda;Popiringidza mibvi yace ikhale yodukaduka.
8. Apite ngati nkhono yosungunuka;Asaone dzuwa monga mtayo,
9. Miphika yanu isanagwire moto waminga,Adzaiuluza, yaiwisi ndi yoyaka.
10. Wolungama adzakondwera pakuona kubwezera cilango:Adzasamba mapazi ace m'mwazi wa woipa.
11. Ndipo anthu adzati, Indedi, pali mphotho kwa wolungama;Indedi, pali Mulungu wakuweruza pa dziko lapansi.