Masalmo 58:7-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Apitetu ngati madzi oyenda;Popiringidza mibvi yace ikhale yodukaduka.

8. Apite ngati nkhono yosungunuka;Asaone dzuwa monga mtayo,

9. Miphika yanu isanagwire moto waminga,Adzaiuluza, yaiwisi ndi yoyaka.

10. Wolungama adzakondwera pakuona kubwezera cilango:Adzasamba mapazi ace m'mwazi wa woipa.

11. Ndipo anthu adzati, Indedi, pali mphotho kwa wolungama;Indedi, pali Mulungu wakuweruza pa dziko lapansi.

Masalmo 58