Masalmo 58:4-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ululu wao ukunga wa njoka;Akunga mphiri yogontha m'khutu, itseka m'khutu mwace.

5. Imene simvera liu la oitana,Akucita matsenga mocenieratu,

6. Tyolani mano ao m'kamwa mwao, Mulungu:Zulani zitsakano za misona ya mkango, Yehova.

7. Apitetu ngati madzi oyenda;Popiringidza mibvi yace ikhale yodukaduka.

Masalmo 58