4. Ululu wao ukunga wa njoka;Akunga mphiri yogontha m'khutu, itseka m'khutu mwace.
5. Imene simvera liu la oitana,Akucita matsenga mocenieratu,
6. Tyolani mano ao m'kamwa mwao, Mulungu:Zulani zitsakano za misona ya mkango, Yehova.
7. Apitetu ngati madzi oyenda;Popiringidza mibvi yace ikhale yodukaduka.