6. Ndipo ndinati, Ha, wina akadandipatsa mapiko onga a njiwaMwenzi nditauluka, ndi kukhaliratu.
7. Onani, ndikadathawira kutari,Ndikadagona m'cipululu.
8. Ndikadafulumira ndipulumukeKu mphepo yolimba ndi namondwe.
9. Aonongeni, Ambuye, gawani lilime lao:Pakuti ndaona ciwawa ndi ndeu m'mudzimo.