Masalmo 55:21-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Pakamwa pace mposalala ngati mafuta amkaka,Koma mumtima mwace munali nkhondo:Mau ace ngofewa ngati mafuta oyenga,Koma anali malupanga osololasolola.

22. Umsenze Yehova nkhawa zako, ndipo Iyeadzakugwiriziza:Nthawi zonse sadzalola wolungama agwedezeke.

23. Koma Inu, Mulungu, mudzawatsitsira ku dzenje la cionongeko:Anthu okhetsa mwazi ndi acinyengo masiku ao sadzafikira nusu;Koma ine ndidzakhulupirira Inu.

Masalmo 55