Masalmo 5:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mverani mau anga, Yehova,Zindikirani kulingirira kwanga.

2. Tamvetsani mau a kupfuula kwanga,Mfumu yanga, ndi Mulungu wanga:Pakuti kwa Inu ndimapemphera,

3. M'mawa, Yehova, mudzamva mau anga;M'mawa, ndidzakukonzerani pemphero langa, ndipo ndidzadikira.

4. Pakuti Inu sindinu Mulungu wakukondwera naco coipaMphulupulu siikhala ndi Inu.

5. Opusa sadzakhazikika pamaso panu:Mudana nao onse akucita zopanda pace.

6. Mudzaononga iwo akunena bodza:Munthu wokhetsa mwazi ndi wacinyengo, Yehova anyansidwa naye.

Masalmo 5