Masalmo 48:3-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Mulungu adziwika m'zinyumba zace ngati msanje.

4. Pakuti, taonani, mafumuwo anasonkhana,Anapitira pamodzi.

5. Anapenya mudziwo, ndipo pamenepo anadabwa;Anaopsedwa, nathawako.

6. Pomwepo anagwidwa nako kunthunthumira;Anamva cowawa, ngati wam'cikuta.

7. Muswa zombo za ku Tarisi ndi mphepo ya kum'mawa.

8. Monga tidamva, momwemo tidapenyaM'mudzi wa Yehova wa makamu, m'mudzi wa Mulungu wathu:Mulungu adzaukhazikitsa ku nthawi yamuyaya.

9. Tidalingalira za cifundo canu, Mulungu,M'kati mwa Kacisi wanu.

10. Monga dzina lanu, Mulungu,Momwemo lemekezo lanu ku malekezero a dziko lapansi:M'dzanja lamanja lanu mudzala cilungamo.

Masalmo 48