Masalmo 45:10-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Tamvera, mwana wamkaziwe, taona, tachera khutu lako;Uiwalenso mtundu wako ndi nyumba ya atate wako;

11. Potero mfumuyo adzakhumba kukoma kwako:Pakuti ndiye mbuye wako; ndipo iwe umgwadire iye.

12. Ndipo mwana wamkazi wa Turo adzafika nayo mphatso;Acuma a mwa anthu adzapempha kudziwika nanu.

13. Mwana wamkazi wa mfumu ngwa ulemerero wonse m'kati mwa nyumba:Zobvala zace nza made agolidi.

14. Adzamtsogolera kwa mfumu wabvala zamawanga-mawanga:Anamwali anzace omtsata adzafika nao kwa inu.

Masalmo 45