Masalmo 44:8-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Mwa Mulungu tidzitamanda tsiku lonse,Ndipo dzina lanu tidzaliyamika kosatha.

9. Koma mwatitaya, ndi kutinyazitsa;Ndipo simuturuka nao makamu a nkhondo athu.

10. Mutibwereretsa kuthawa otisautsa:Ndipo akudana nafe adzifunkhira okha.

11. Mwatipereka ngati nkhosa zoyenera kuzidya;Ndipo mwatibalalitsa mwa amitundu.

12. Mugulitsa anthu anu kwacabe,Ndipo mtengo wace simupindula nao.

Masalmo 44