Masalmo 44:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Mulungu, tidamva m'makutu mwathu, makolo athu anatisimbira,Za nchitoyo mudaicita masiku ao, masiku akale.

2. Inu munapitikitsa amitundu ndi dzanja lanu, koma iwowa munawaoka;Munasautsa mitundu ya anthu, ndipo munawaingitsa,

3. Pakuti sanalanda dziko ndi lupanga lao,Ndipo mkono wao sunawapulumutsa:Koma dzanja lanu lamanja, ndi mkono wanu, ndi kuunika kwa nkhope yanu.Popeza munakondwera nao,

4. Inu ndinu mfumu yanga, Mulungu:Lamulirani cipulumutso ca Yakobo.

5. Mwa Inu tidzakankhira pansi otsutsana nafe:M'dzina lanu tidzapondereza akutiukira ife.

6. Pakuti sinditama uta wanga,Ndipo lupanga langa silingandipulumutse.

7. Koma Inu munatipulumutsa kwa iwo akutsutsana nafe,Ndipo akudana nafe, mudawacititsa manyazi.

Masalmo 44