13. Koma ine, monga gonthi, sindimva;Ndipo monga munthu wosalankhula, sinditsegula pakamwa panga.
14. Inde ndikunga munthu wosamva,Ndipo m'kamwa mwanga mulibe makani.
15. Pakuti ndikuyembekezani Inu, Yehova;Inu mudzayankha, Ambuye Mulungu wanga.
16. Pakuti ndinati, Asakondwerere ine:Pakuterereka phazi langa, asadzikuze pa ine.
17. Ndafikana potsimphina;Ndipo cisoni canga ciri pamaso panga cikhalire.
18. Pakuti ndidzafotokozera mphulupulu yanga;Nditenga nkhawa cifukwa ca chimo langa.