Masalmo 38:13-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Koma ine, monga gonthi, sindimva;Ndipo monga munthu wosalankhula, sinditsegula pakamwa panga.

14. Inde ndikunga munthu wosamva,Ndipo m'kamwa mwanga mulibe makani.

15. Pakuti ndikuyembekezani Inu, Yehova;Inu mudzayankha, Ambuye Mulungu wanga.

16. Pakuti ndinati, Asakondwerere ine:Pakuterereka phazi langa, asadzikuze pa ine.

17. Ndafikana potsimphina;Ndipo cisoni canga ciri pamaso panga cikhalire.

18. Pakuti ndidzafotokozera mphulupulu yanga;Nditenga nkhawa cifukwa ca chimo langa.

Masalmo 38