Masalmo 35:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Tsutsanani nao iwo akutsutsana nane, Yehova:Limbanani nao iwo akulimbana nane.

2. Gwirani cikopa cocinjiriza, Ukani kundithandiza.

3. Sololani nthungo, ndipo muwatsekerezere kunjira akundilondola:Nenani ndi moyo wanga, Cipulumutso cako ndine.

4. Athe nzeru nacite manyazi iwo akufuna moyo wanga:Abwezedwe m'mbuyo nasokonezeke iwo akundipangira ciwembu.

5. Akhale monga mungu kumphepo,Ndipo mngelo wa Yehova awapitikitse.

6. Njira yao ikhale ya mdima ndi yoterera,Ndipo mngelo wa Yehova awalondole.

Masalmo 35