1. Pfuulani mokondwera mwa Yehova, inu olungama mtima:Oongoka mtima ayenera kulemekeza.
2. Yamikani Yehova ndi zeze:Myimbireni ndi cisakasa ca zingwe khumi.
3. Mumyimbire Iye Nyimbo yatsopano;Muyimbe mwaluso kumveketsa mau.
4. Pakuti mau a Yehova ali olunjika;Ndi nchito zace zonse zikhulupirika.