5. Ndipereka mzimu wanga m'dzanja lanu:Mwandiombola, Inu Yehova, Mulungu wa coonadi.
6. Ndikwiya nao iwo akusamala zacabe zonama:Koma ndikhulupirira Yehova.
7. Ndidzakondwera ndi kusangalala m'cifundo canu:Pakuti mudapenya zunzo langa;Ndipo mudadziwa mzimu wanga mu nsautso yanga: