Masalmo 31:15-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Nyengo zanga ziri m'manja mwanu:Mundilanditse m'manja a adani anga, ndi kwa iwo akundilondola ine.

16. Walitsani nkhope yanu pa mtumiki wanu:Mundipulumutse ndi cifundo canu.

17. Yehova, musandicititse manyazi; pakuti ndapfuulira kwa Inu:Oipa acite manyazi, atonthole m'manda.

18. Ikhale yosalankhula milomo ya mabodza,Imene imalankhula mwacipongwe pa olungama mtima,Ndi kudzikuza ndi kunyoza.

Masalmo 31