1. Ndidzakukwezani, Yehova; pakuti mwandinyamutsa,Ndipo simunandikondwetsera adani anga,
2. Yehova, Mulungu wanga,Ndinapfuulira kwa Inu, ndipo munandiciritsa.
3. Yehova munabweza moyo wanga kumanda:Munandisunga ndi moyo, kuti ndingatsikire kudzenje.
4. Yimbirani Yehova, inu okondedwa ace,Ndipo yamikani pokumbukila ciyero cace.