6. Kuturuka kwace lituruka kolekezera thambo,Ndipo kuzungulira kwace lifikira ku malekezero ace:Ndipo kulibe kanthu kobisalira kutentha kwace.
7. Malamulo a Yehova ali angwiro, akubwezera moyo;Mboni za Yehova ziri zokhazikika, zakuwapatsa opusa nzeru;
8. Malangizo a Yehova ali olungama, akukondweretsa mtima:Malamulo a Yehova ali oyera, akupenyetsa maso.