Masalmo 18:42-45 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

42. Pamenepo ndinawapera ngati pfumbi la kumphepo;Ndinawakhuthula ngati matope a pabwalo.

43. Mwandipulumutsa pa zolimbana nane za anthu;Mwandiika mutu wa amitundu;Mtundu wa anthu sindinaudziwa udzanditumikira.

44. Pakumva m'khutu za ine adzandimvera:Alendo adzandigonjera monyenga.

45. Alendo adzafota,Nadzaturuka monjenjemera m'ngaka mwao.

Masalmo 18