Masalmo 18:21-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Pakuti ndasunga njira za Yehova,Ndipo sindinacitira coipa kusiyana ndi Mulungu wanga.

22. Pakuti maweruzo ace onse anali pamaso panga,Ndipo malemba ace sindinawacotsa kwa ine.

23. Ndipo ndinakhala wangwiro ndi iye,Ndipo ndinadzisunga wosacita coipa canga.

24. Ndimo anandisudzulira Yehova monga mwa cilungamo canga,Monga mwa kusisira kwa manja anga pamaso pace.

25. Pa wacifundo mukhala wacifundoPa mumthu wangwiro mukhala wangwiro;

Masalmo 18